Joyce Chitsulo
Joyce Chitsulo
Hon Joyce Chitsulo
Mwanza West MP
Vote Now

Wachiwiri kwa nduna ya maboma ang'ono Joyce Chitsulo apempha mafumu kuchilimika pa chitukuko.

None
Social Development

Wachiwiri kwa nduna ya maboma ang'ono Joyce Chitsulo apempha mafumu kuchilimika pa chitukuko.

Wachiwiri kwa nduna yamaboma aang'ono, a Joyce Chitsulo, apempha mafumu kuti akhale patsogolo kulondoloza ntchito za chitukuko komanso ndalama zomwe boma likupereka kumadera  ndicholinga choti masomphenya a chitukuko  omwe mtsogoleri wadziko lino, Dr Lazarus Chakwera alinawo, atheke m’dziko mini. 

A Chitsulo anena izi  pa mwambo okweza GVH Matanda kukhala Sub Traditional Authority Matanda m’dera la Senior Chief Chitukula m’boma la Lilongwe. 

Iwo ati boma lakhazikitsa ndondomeko monga za Mtukula Pakhomo, ndalama zakudera za Constituency Development Fund ngakhalenso zangongole, mwazina, choncho ndipofunika kuti mafumu adzionetsetsa kuti ndalama zikugwira ntchito zoyenera komanso kukagogoda m'makomo moyenera ngati anthu awo sakupindula.  

Iwo atinso mafumuwa ali ndi udindo waukulu pogwirana manja ndi boma pothana ndi mchitidwe wa ziphuphu  poonetsetsa kuti thandizo lomwe boma likupereka akuligawa kwa oyenera. 

Mmawu ake, Senior Chief Kalumbu ati ntchito ya mafumu ndi kuthandizana ndi boma kubweretsa chitukuko, bata, mtendere komanso chilungamo choncho apempha mafumuwa kuti agwire ntchito limodzi ndi boma.