Joyce Chitsulo
Joyce Chitsulo
Hon Joyce Chitsulo
Mwanza West MP
Vote Now

Veteran MCP guru, Manjamkhosi cheers Deputy Minister Chitsulo

None
Social Development

Veteran MCP guru, Manjamkhosi cheers Deputy Minister Chitsulo


Mkhalakale pa ndale m’dziko muno, a Hilda Manjamkhosi, lero lachinayi pa 22 May 2025, anakacheza ndi wachiwiri kwa nduna ya maboma ang'ono omwenso ndi phungu wadera lakuzambwe m’boma la Mwanza, a Joyce Chitsulo, omwe adachita ngozi masiku apitawa.

Poyankhula ndi MBC munzinda wa Lilongwe, a Manjamkhosi omwe adakhalapo mkulu wa amayi ku chipani cha Malawi Congress (MCP) anati anachiona chanzeru kuti akawaone a Chitsulo ngati mbali imodzi yowalimbikitsa.

A Manjamkhosi anapita limodzi ndi mlangizi wa Prezidenti pa nkhani za amayi mchipani cha MCP, a Dorothy Chirambo.

Ndipo a Chitsulo ayamika anthu osiyanasiyana  omwe akhala akumakawazonda.

Malinga ndi a Chitsulo, pali chiyembekezo kuti chikhakha chomwe adawaika adzachichotsa pa 2 June 2025, ndipo kwakukulu akuyamika Mulungu chifukwa cha zokoma zomwe wawachitira.